Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 239
Paphata pa Chichewa
kutero ndiye kuti mankhwalawo asuluka. Koma ndi
zikhulupiriro chabe zimene anthu ambiri akuda amakhala
nazo.
Chitsanzo: Ndatopa kuzungulira m’zipatala,
mundifufuzire mankhwala achikuda.
(b) Mankwala ochokera kumitengo.
Chitsanzo: Kale kulibe zipatala tinkadalira kwambiri
mankhwala achikuda.
Mankhwala azitsamba: Mankhwala ochokera ku mitengo,
angatanthauzenso mankhwala ochokera kwa asing’anga,
mankhwala achikuda.
Chitsanzo: Anthu a chipembedzo chimenechi amakana
kumwa mankhwala azitsamba.
Manong’onong’o:
(a) Mphekesela, nkhani imene anthu akukamba
mwachinsinsi.
Chitsanzo: Pamudzi pano pakumveka manong’onong’o
onena kuti mwana uja si wawo.
(b) Kuyankhula chapansipansi.
Chitsanzo: Ndani akupanga manong’onong’o uko!
Manong’onong’o: Mphekesera, nkhani imene ikumveka,
nkhani imene anthu akukamba.
Chitsanzo: Kodi manong’onong’o akumvekawa ndi a
ndani?
Manthongo: Zoipa zimene zimasonkhana m’mbali mwa
maso munthu ukamadzuka kapena ukamadwala maso.
Chitsanzo: Tamuchotsani manthongo mwanayo!
Manthu wa mavuto: Mavuto aakulu.
Chitsanzo: Chaka chino tikumana ndi manthu wa mavuto.
Manyong’olomeza: Tizakudya tokoma.
Chitsanzo: Andigulira manyong’olomeza.
Mapazi potopoto: Mawuwa amanenedwa ponyoza mmene
munthu akuyendera.
238