Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 237
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: (1) Sindidzamugulanso, amakonda kuchita
malonda a mphaka. (2) Mukuti ndigule katunduyo
ndisanamuone. Amenewatu ndi malonda a mphaka.
Malovu m’kamwa nde: Kusowa chonena.
Chitsanzo: Atamufunsa anangoti malovu m’kamwa nde!
Maluli: Kusaphonya.
Chitsanzo: Pamudzi pano pali anyamata amaluli, saponya
mwala pachabe.
Maluwa a dziko: Akazi
Chitsanzo: Mukamangoti maso m’mwamba mupita,
akazitu ndi maluwa a dziko! Simungawakwanitse onse.
Mambala: Tambwali, wakuba.
Chitsanzo: Munthu ameneyu ndi mambala.
Mamulumuzana: Anthu wachikulire, olemekezeka.
Chitsanzo: Kumsonkhanowo kunabwera mamulumuzana.
Mana: Zinthu zaulere. Mawuwa anachokera ku Mana
yemwe ankagwa m’chipululu pamene Aisiraeli ankapita
ku Kanani.
Chitsanzo: Chaka chino mana watigwera.
Mandevu: Munthu wandevu zambiri.
Chitsanzo: Mwawaona a mandevu aja?
Manga lamba: Kulimba nazo, kulimbikira.
Chitsanzo: Amene akufuna kupambana ayenera kumanga
lamba.
Manga m’phukusi: Kukubisira.
Chitsanzo: Zimene anafotokoza sizimamveka bwinobwino,
wangotimanga m’phukusi.
Manga mlaza m’maso: Kulimba mtima, kusachita
manyazi.
Chitsanzo: Nditaona kuti anthu akundiseka,
ndinangomanga mlaza m’maso.
236