Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 232
Paphata pa Chichewa
Madoda: Anthu akuluakulu, anthu audindo.
Chitsanzo: Kodi madoda ali panjawa abwera kudzatani?
Madyeramphoto: Anthu okonda kupereka kapena
kulandira ziphuphu, anthu omwe amafuna kudya zaulere,
anthu omwe amachita zautambwali.
Chitsanzo: Anthu a khalidwe la umadyeramphoto
akuchuluka masiku ano.
Madyerero: Phwando.
Chitsanzo: Kwathu kuli madyerero.
Madzalamphuno: Munthu woyankhula zosamveka.
Chitsanzo: Zoona mungabwere ndi madzalamphunoyu.
Madzi achita katondo: Pavuta, zasokonekera.
Chitsanzo: Nditaona kuti madzi achita katondo,
ndinangochokapo.
Madzi afika m’khosi: Zinthu zavuta.
Chitsanzo: (1) Ndikuona kuti zitivuta tikayamba ku-
chitapo kathu madzi atafika m’khosi. (2) Tiyeni tisamuke
madzi asanafike m’khosi.
Madzi akali m’nkhongono: Zisanavute.
Chitsanzo: (1) Ndi bwino tidziwiretu chochita madzi akali
m’nkhongono. (2) Tiyeni tithane ndi vutoli madzi akali
m’nkhongono.
Madzi m’kulubza mchenga upita pamwamba: Kunena
zinthu mwachinsinsi.
Chitsanzo: Sitimadziwa kuti madzi m’kulubza mchenga
upita pansi. Onsewa akudziwa ndithu.
Mafana: Ana, anthu osadziwa zambiri.
Chitsanzo: Kodi mafana aja ali kuti?
Mafilimu: Munthu yemwe amachita zautamwali ama-
munena kuti ndi wamafilimu.
Chitsanzo: Mwanayu ndi wamafilimu.
231