Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 231

Paphata pa Chichewa M’mimba ndi n’chipala: Chipala ndi malo omwe anthu amasulirapo zinthu zosiyanasiyana monga makasu, nkhwangwa, mipeni ndi zina. Chifukwa choti pachipala pakhoza kupangidwa chilichonse, amayerekezera m’mim- ba kuti munthu akhoza kubereka mwana wovuta ndi wabwino ndi mimba imodzi yomweyo. Chitsanzo: Ukakaona kusiyana kwa khalidwe lawo ukamvetsadi kuti m’mimba ndi m’chipala. M’mwamba: Mumtengo. Chitsanzo: Osamakwera m’mwamba. M’thengo mudalaka njoka: Kwanu ndi kwanu, ngakhale patatenga nthawi yaitali bwanji umadzabwererako. Chitsanzo: Asiyeni abwerako, m’thengo mudalaka njoka. M’tupatupamu: Mawu amene amanenedwa ngati munthu sakufuna kunena kumene wapeza zinazake. Mawuwa ndi ofanana ndikunena kuti “kwinakwake.” Chitsanzo: “Mwazitenga kuti ndalamazi?” “M’tupatupamu.” Mabebi: Mawu omwe achinyamata amanena akamanena za akazi. Chitsanzo: Mabebi ambiri ndi a milomo yokhala ngati achita kusongola. Mabonzo: Mafupa. Chitsanzo: Ndinapeza atamaliza ndiwo zonse, moti ndinangopeza mabonzo okhaokha. Machawi: Changu. Chitsanzo: Chitani machawi tingachedwe. Madala: Bambo wachikulire. Chitsanzo: Madala andituma kuti ndikawagulire mowa. Madobadoba: Anthu omwe amangoyendayenda m’tauni osadziwika bwino zochita zawo. Chitsanzo: M’tauni muno muli madobadoba omwe cholinga chawo n’kupusitsa anthu. 230