Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 23
Paphata pa Chichewa
Chabwalo: Ndalama zomwe anthu amalipira kuti mlandu
wawo uweruzidwe.
Chitsanzo: Kuti tiweruze mlanduwu, perekani kaye
chabwalo.
Chadza ndi yani? Mawu omwe anthu amanena podabwa
chifukwa chake wina wachita zinazake zachilendo.
Chitsanzo: Chadza ndi yani kuti mulowe m’nyumbamu
ndi masilipasi?
Chafutambuyo: Mobwerera kumbuyo.
Chitsanzo: Akuyenda chafutambuyo.
Chagona apa: Pamene pali nkhani.
Chitsanzo: Chinsinsi chake chagona apa.
Chagona pati: Pamene pali nkhani.
Chitsanzo: (1) Kodi chinsinsi chake chagona pati? (2) vuto
lagona pati?
Chakachadza: Munthu amene amati akabereka mwana,
mwanayo amamwalira.
Chitsanzo: Akazi anuwa ndi a chakachadza.
Chakachika: Kusowa ndalama, kusauka kwambiri.
Chitsanzo: (1) Atsikana akuno akufuna anyamata
okongola m’nthumba, osati ochakachika. (2) Amukana
chifukwa ndi wochakachika.
Chakhola: Chiweto chimene munthu amapereka kwa eni
khola pothokoza kuti awawetera ziweto zawo m’khola
lawo.
Chitsanzo: Musanatenge mbuzi zanu, perekani kaye
chakhola.
22