Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 229
Paphata pa Chichewa
Lungama: Kukhala munthu wopanda cholakwa,
kusalakwitsa kanthu.
Chitsanzo: Padziko lapansi palibe munthu wolungama.
Lunjika: Yenda moloza chinachake, loza chinthu,
yang’ana chinthu, ponya moloza chinachake.
Chitsanzo: amayenda molunjika ineyo.
Luntha: Khama.
Chitsanzo: Sukulu imafuna munthu waluntha.
Lusifala: Munthu woipa kwambiri.
Chitsanzo: Sindimadziwa kuti bambowa ndi Lusifala
Lusifala: Munthu woipa, Satana.
Chitsanzo: (1) Munthu amene uja ndi lusifala. (2) Lusifala
anathamangitsidwa kumwamba.
Luzi m’nkhosi: Kukalamba, makwinya a ukalamba.
Chitsanzo: Amayi okongola aja anangotsala ndi luzi m’nk-
hosi.
228