Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 228

Paphata pa Chichewa Luma chiputu (gwira chiputu): Kanirira. Chitsanzo: (1) Ndinamuuza kuti atuluke m’nyumbamo koma akuluma chiputu. (2) Mkamwini uja anagwira chiputu, safuna kuchoka pamudzi paja. Luma khutu (tsina khutu): Kuulula pang’ono. Chitsanzo: (1) Kodi anakutsinani khutu zokhudza ulendo uja? (2) Andiluma khutu za nkhaniyi ndi achemwali anga aja. Luma mano: (a) Kufa utadwala. Chitsanzo: Sizimakhala zodandaulitsa kwambiri nkhalam- ba ikaluma mano. (b) Kuchita khama (kunyindirira). Chitsanzo: Pogwira ntchito umafunika kuluma mano. Lumana chala: Kupangana kuchita chinthu chimodzi. Chitsanzo: Ngati tikufuna zitiyendere, tifunika tilumane chala. Lumana: Kudana. Chitsanzo: (1) Akagwirizana alekeni, mawa adzalumananso. (2) Mabwenzi apamtima aja analumana. Lumira mlomo: Limbikira. Chitsanzo: Ntchitoyi ndi yovuta moti ndi yofunika kulumira mlomo. Lumo: Mpeni, chinthu chakuthwa. Chitsanzo: Lamucheka ndi lumo. Lumphitsa mpanda: Kuchititsa kuti athawe. Chitsanzo: Akuba anabwera aja awalumphitsa mpanda. Lungalunga: Munthu wabwinobwino wopanda chilema. Chitsanzo: Ukakhala walungalunga osamatha mawu, chilemba chimachita kubwera. Lungalunga: Munthu wopanda chilema. Chitsanzo: Lungalunga n’kubadwa, chilema chidza kuusa- na. 227