Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 227

Paphata pa Chichewa Lowa m’vwivwi: Kulowa m’gulu. Chitsanzo: Wakubayo ataona kuti anthu ayamba kumuthamangitsa, anangolowa m’vwivwi ndipo sanaonekenso. Lowa: Kumuyesa mnzako kapena munthu wina, kusalemekeza munthu, kunyoza munthu. Chitsanzo: Sindimafuna kuti munthu azindilowa. Lowe: Malo odikha madzi, malo otsika. Chitsanzo: Mpunga umachita bwino palowe. Lowerera: (a) Kusokonekera, kukhala ndi khalidwe loipa, kusamva. Chitsanzo: Mwanayu ndi wolowerera. (b) Kusowa, kuzemba, kulowa m’chigulu. Chitsanzo: Wangolowerera m’chigulu. Lowetsa mutu m’phiko: Kukhala ngati sukuona. Chitsanzo: Pamene ndimafuna ndimukodele anangolowetsa mutu m’phiko. Loza chala (veka mlandu): Kuimba munthu wina mlan- du. Chitsanzo: Mukayambana m’banja, zimakhala bwino kuti mungokambirana m’malo momalozana chala (momaveka wina mlandu). Loza ndege ndi chala: Nyada. Chitsanzo: (1) Akazi awo aja anasintha kwambiri moti masiku ano amaloza ndege ndi chala. (2) Kodi tikalemera ndiye tiziloza ndege ndi chala? Loza nthiko: Kumbukira kumudzi. Chitsanzo: Atakhala kwa miyezi ingapo, bamboyo analoza mthiko. Luma chala: Khala duu osanena kanthu, kusaulura nkhani. Chitsanzo: (1) Atamva nkhaniyo ndinangoluma chala. (2) Ukawamva akukamba nkhani imeneyi, ungoluma chala. 226