Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 225
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: Ataona kuti zavuta, analiyatsa liwiro la
mtondowadooka.
Liwiro: Wachimasomaso, wadama, wokonda amuna
kapena akazi.
Chitsanzo: Mkazi akakhala wa liwiro, amuna
samufunsira.
Liwongo: Mlandu.
Chitsanzo: Sindikufuna kuchita nawo zimenezi, ndikuopa
kukhala ndi liwongo la magazi.
Lizita: Khama loopsa.
Chitsanzo: (1) Munthu uyu ndi wa lizita. (2) Kukhala ndi
lizita n’kukhalanso mbuli ndi nsakanizo woopsa.
Lodza: Mawu amenewa amagwiritsidwa ntchito ponena za
zikhulupiriro zomwe anthu a ku Africa kuno amakhala
nazo zoti anthu amatha kuchititsa kuti mnzawo afe
kapena akumane ndi tsoka linalake. Angatanthauze ku-
chita mankhwala kuti wina adwale.
Chitsanzo: Ukufuna uyambane ndi ine eti, ndikuphwan-
yatu! Akulodza eti?
Lola opanda mano: Mwayi kugwera anthu opanda omwe
sakuufuna.
Chitsanzo: Taonani katundu apezayu? Koma zoonadi
chimanga chimalola opanda mano.
Lololo: Zambirimbiri.
Chitsanzo: Ndalama ndili nazo lololo.
Longa diso momwe: Thandiza kwambiri.
Chitsanzo: Mwana ameneyu ukamusamalira bwino
adzakulonga diso momwe.
Lowa chamwaka: Kudwaladwala.
Chitsanzo: Amalume sakupeza bwino, alowa chamwaka.
Lowa libolonje (njobwe):
(a) Kudwaladwala.
224