Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 222

Paphata pa Chichewa Laponda diwa: Kuchita mwayi. Chitsanzo: Laponda diwa, ntchito ikumasowa masiku ano! Laponda lamphawi: Kuchita mwayi. Chitsanzo: Atandiitanira nsimayo, ndinangoti laponda lamphawi! Lasa: (a) Kunena mfundo yomveka. Chitsanzo: Apo ndiye mwalasatu, mfundo koma imeneyo. (b) Kunena mawu opweteka. Chitsanzo: Mawu mwayankhulawo andilansa mumtima. (c) Kupereka mimba. Chitsanzo: (1) Mwamuna akapereka mimba timati walasa. (2) Mnyamata ankamuderera ujatu walasa. Lawira: (a) Kutsanzika. Chitsanzo: Ndikupita kukawalawira achimwene kuseriku. (b) Kulawa chinthu m’malo mwa munthu wina. Chitsanzo: Bwerani tikulawireni ngati zili ndi mchere. (c) Kunyamuka m’mawa kwambiri. Chitsanzo: Mawa ndilawira kwambiri. Ledzera ndi mphamvu: Chita nkhanza. Chitsanzo: Wolamulira akaledzera ndi mphamvu ama- yamba kugwira anthu n’kumakadyetsera ng’ona. Lemba: Pusitsa, dyetsa njomba. Mawuwa amachokera ku zimene wosewera mpira amachita akamadyetsa njomba anzake. Chitsanzo: Musadzampatsenso ndalama zanu, adzaku- lembani. Lembam’madzi: Lephera. Chitsanzo: Walembam’madzi, amaganiza angandipusitse. Lemberana chimfine: Kumana onse a pachibale. Chitsanzo: Anthu onse a pamudzipa akulemberana chimfine lero. 221