Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 220

Paphata pa Chichewa anzanu onse anakwatiwa ndi pantchafu. Kwawo kapande: Zipitani kwanu. Chitsanzo: Kwada tsopano, kwawo kapande. Kwaya wausiku (eko wausiku): Kupatsa munthu pang’ono. Chitsanzo: Ukamapereka chinthu kwa munthu osamachita kwaya wausiku ngati anakupempha. Kwayauwotche: Matenda opatsirana pogonana. Chitsanzo: (1) Mwana wa Anamasina anatenga kwayau- wotche. (2) Ukamangoti maso m’mwamba anthu akupatsa kwayauwotche. Kwenya: Gwira malaya a munthu pomuopseza. Chitsanzo: Anamukwenya mpaka lamba kuduka. Kwera chitunda: Mawuwa amanenedwa munthu ak- amakumana ndi mavuto. Chitsanzo: Anzanu ajatu akukwera chitunda. Kwera pachulu: Kulalata, kutukwana. Chitsanzo: Akapanda kubweretsa ndimukwerera pachulu. Kwera paudindo: Kupatsidwa udindo waukulu. Chitsanzo: Anthu amene amakwera paudindo amakhala olimbikira. Kweza changa m’mwamba: Pulumutsa. Chitsanzo: Ntchito anatiuza kuti tikagwireyo inali yovuta. Mwamwayi kapitawo anandiuza kuti anthu akwanira moti anakweza changa m’mwamba. Kwidzinga: Mawu okokomeza onena za munthu amene wamangidwa atapalamula. Chitsanzo: Wakubayo anamukwidzinga ndi unyolo. Kwingwinyala: Chita manyazi. Chitsanzo: (1) Atangomuseka, nthawi yomweyo anakwingwinyala. (2) Bodza lako likaonekera umangokwingwinyala. 219