Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 218

Paphata pa Chichewa Kuzisiya: Kulephera, kugonja. Chitsanzo: Osewera amatama aja azisiya. Kuzonda: (a) Kudana ndi munthu, kuzondana ndi kusaonana bwino. Chitsanzo: Anthu amenewa amandizonda. (b) Kukaona anthu. Chitsanzo: (1) Amene anabwera kudzatizonda ndi am- alume awo. (2) Ndinapita kukazonda matenda. Kuzondotsa: Kulozetsa chinthu pansi. Chitsanzo: (1) Mabukuwa mwawaika mozondoka. (2) Mwazondotsa, mituyi izikhala m’mwamba. Kuzuka: (a) Munthu wamtali komanso wamkulu thupi. Chitsanzo: Mtsikana wake ndi wozuka. (b) Kuchoka mumthaka. Chitsanzo: Chinakwa sichichedwa kuzuka. Kuzula minga ya pamsana: Thandiza kwambiri. Chitsanzo: Amenewa ndi amene anandizula minga ya pamsana zitandivuta chaka chatha. Kuzuna: Kukoma kwambiri, kusangalatsa, kutsekemera kwambiri. Chitsanzo: (1) Nkhani mwalembayi ndi yozuna. (2) Uchi umazuna. Kuzungulira mutu: Kuchita misala, kusaganiza bwino. Chitsanzo: (1) Kodi ndiwe wozungulira mutu eti? (2) Ana awo onse ndi ozungulira mitu. Kuzunguza: Kuvutitsa, kuvuta kwa chinthu. Chitsanzo: (1) Mwanayu ndi wozunguza. (2) Samuyi ndi yozunguza. Kuzunguzika: Kusokonezeka. Chitsanzo: Ngoziyo itachitika, bamboyo anazunguzika maganizo. 217