Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 217

Paphata pa Chichewa (b) Kukhazikika. Chitsanzo: Sitifuna kuti alendo azizika mizu pakhomo pano Kuzilala: Kufooka, kuzima. Chitsanzo: (1) Nkhosa zambiri za tchalitchi ichi zinazilala. (2) Moto uja wazilala. Kuzimiratu: Kugoneratu. Chitsanzo: Anabwera usiku kwambiri moti ndinali nditazimiratu. Kuzimiririka: Kusaonekanso, kutsenjira. Chitsanzo: (1) Pamene ndimazindikira kuti wandibera n’kuti munthuyo atazimiririka. (2) Ndinamuona akubwera koma kenako anangozimiririka. Kuzimuka: Kumvetsera Mawu a Mulungu kapena nyimbo zauzimu. Chitsanzo: Tipite kutchalitchi tikazimuke. Kuzingwa kwa Kalulu kukapsa: Kutanganidwa kosowa nako chochita. Chitsanzo: Kumenekutu ndiye kuzingwa kwa kwalulu kukapsa. Kuzingwa: Kusokonezeka, kusowa pogwira. Chitsanzo: (1) Galu wangayu ndi amene anamuzigwitsa kalulu uja. (2) Ukazigwa vuto lililonse limakhala ngati phiri. Kuzipulumutsa zibakera: Kumenya munthu ndi zibakera. Chitsanzo: Anthu achibwibwi sachedwa kuzipulumutsa zibakera ukamawauza zachihatahata. Kuzisaka: Kufufuza ndalama. Chitsanzo: (1) Atsikana a masiku ano ndi ozisaka. (2) Kungodikira kapena kuyenda ulendo popanda kanthu, kulephera. 216