Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 214
Paphata pa Chichewa
(b) Kugulidwa ndi anthu ambiri.
Chitsanzo: Chimangachi chikuyenda malonda.
Kuyenda modzithinula: Kuyenda monyada.
Chitsanzo: Akabwera kumene kutauni amayenda
modzithinula.
Kuyenda mwamdidi: Kuyenda mopanda choopa.
Chitsanzo: Akakatamuka amayenda mwamdidi.
Kuyenda n’kuvina: Sungadziwe kuti mawa ukapezeka
kuti, kuyenda sikudziwika.
Chitsanzo: (1) Ukakumana ndi munthu, osamamuchitira
chipongwe chifukwa kuyenda n’kuvina. (2) Mwina tidza-
kumananso, kuyenda n’kuvina.
Kuyenda ndawala: Kuyenda mofulumira.
Chitsanzo: Tiyeni tiziyenda ndawala tingachedwe.
Kuyenda ndi dziko (kuthamanga ndi dziko): Kuchita
zonse zimene zikuchitika m’dzikoli, kuchita makhalidwe
oipa.
Chitsanzo: Amayenda ndi dziko, lero lamutembenukira.
Kuyenda ndi mdidi: Kuyenda mopanda mantha.
Chitsanzo: Akakhala nazo ndalama amayenda ndi m’didi.
Kuyenda pakhomo pali pululu: Kuyenda osatseka zipi,
lisani.
Chitsanzo: Abwana athu amayenda pakhomo pali pululu.
Kuyenda pamlatho waphesi: kuyaluka chifukwa cha
khalidwe loipa.
Chitsanzo: Akuyenda pamlatho waphesi chifukwa cha
khalidwe lake lachisembwere.
Kuyenda punzipunzi: Kuyenda modzikoka, kuyenda
ngati ukufuna kugwa, kudzandira.
Chitsanzo: Agogo anabwera kuno akuyenda punzipunzi
chifukwa cha ukalamba.
213