Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 211

Paphata pa Chichewa Kuyamika wamoto: Kuyamikira mofulumira usanaone khalidwe lenileni. Chitsanzo: Aliyense ankanena zabwino za munthu ameneyu, koma ankayamika wamoto. Kuyang’ana ndi diso loipa: Kuyang’ana munthu momuzonda, mosonyeza kuti umadana naye. Chitsanzo: Masiku ano akumandiyang’ana ndi diso loipa. Kuyangalayangala: Kuyendayenda. Chitsanzo: Sagwira ntchito, amangokhalira kuyangalayangala m’taunimu. Kuyankha mosisitika: Kuyankha mosatsimikiza, kuyankha motsika kwambiri. Chitsanzo: Atawafunsa ngati zinali zoona anayankha mo- sisitika. Kuyankha mwala: Kuyankha mwano. Chitsanzo: (1) Mayiyo anamupeza akusetekera m’manja. Atamuuza kuti akuchitawo ndi uve, anamuyankha mwa- la. (2) N’chifukwa chiyani masiku ano ukumangondi- yankha mwala? Kuyankha ziphaliwali: Kuyankha mwano. Chitsanzo: Nditamufunsa amangondiyankha ziphaliwali. Kuyankhula chidamula: Kuyankhula mongodula, zosamveka. Chitsanzo: Ndikakumana nawo akumangoyankhula chidamula. Kuyankhula Chigiriki: Kuyankhula zosamveka. Chitsanzo: Enawatu amaona ngati mukuyankhula Chigiriki. Kuyankhula chikapaya: Kuyankhula zosamveka, mozungulira. Chitsanzo: Ukamafunsira sumafunika kumayankhula chikapaya. 210