Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 210

Paphata pa Chichewa Kuyabwa: (a) Kunyong’onyeka kapena kusafuna kukhala pansi. Chitsanzo: Bibida ndi amene amawalowa m’thumba, moti akapeza ndalama pakhomo pano pamawayabwa. (b) Kuvutitsa. Chitsanzo: Abwera tsopano, akufuna atiyabwe! Kuyabwidwa ndi chitedze: Kupalamula. Chitsanzo: Samadziwa kuti akuputa mavu nkhomola moti chitedze chinamuyabwa. kuyaka ndi nkwiyo: Kupsa mtima kwambiri. Chitsanzo: Ndinawapeza akuyaka ndi nkwiyo. Kuyaka: Kuledzera. Chitsanzo: Ndinakumana nawo atayakiratu. Kuyala masamba auma: Dikirira nthawi yaitali. Chitsanzo: Anakhala pamenepo mpaka masamba auma. Kuyala nkhani yonse: Kufotokoza zonse mwatsatanetsa- tane. Chitsanzo: Bwerani ndikuyalireni nkhani yonse. Kuyala udzu pamimba: Kupusitsa munthu. Chitsanzo: Akungofuna kukuyala udzu pamimba. Kuyaluka: Kuchita manyazi kapena kupusa. Chitsanzo: (1) Mukamangouza aliyense nkhani imeneyi muwayalutsa amuna anu aja. (2) Mukamalimbana nawo akuyalutsani. (3) Mukagwidwa muyaluka. Kuyalutsa: Kuulula zinthu zachinsinsi, kunyoza kothera- tu. Chitsanzo: (1) Zochita za mayi aja zimayalutsa amuna awo. (2) Koma ndiye wayalukatu! Kuyambukira: Kukukhudza, kuyamba kuchita zinazake. Chitsanzo: (1) Makhalidwe oipawa akuyambukirani. (2) Zo- chita za makolo zimayambukira ana. 209