Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 21
Paphata pa Chichewa
Bwezera phala kum’kobwe: Kusathokoza, kupanda
pabwino.
Chitsanzo: Zimene mukuchitazitu sizikuthandizani.
Simukudziwa kuti mukubwezera phala kum’kobwe?
Bwira dothi:
(a) Kulephera.
Chitsanzo: Tikamamuuza kuti azilimbikira amatiyesa
ankhanza, lero si izi wabwira dothi!
(b) Kuchimwa.
Chitsanzo: Munthu wachitsanzo chabwino uja anabwira
dothi mumpingo.
(c) Kugwa pansi.
Chitsanzo: Amathamanga ndipo wagwa n’kubwira dothi.
Bwitibwiti: Zonona, za mafuta ambiri.
Chitsanzo: Ndiwo zake zinali za bwitibwiti.
Bwitikiza: Kudzoza (kupaka) mafuta ambiri kapena
zinthu zina.
Chitsanzo: Ali ndi khungu ngati la ng’ona moti kuti
awaleko amafunika kudzibwitikiza m’mafuta.
Bwize: Munthu wakuba.
Chitsanzo: Samalani, kwabwera bwize.
Bzala chinangwa: Kumwalira. Mawuwa anabwera
chifukwa munthu akabzala chinagwa, osati mtengo,
chinangwacho chimangowola.
Chitsanzo: Mkhalakale zonse zidabzala chinangwa.
Bzala ufa: Kunama.
Chitsanzo: (1) Ndinachita kudziwiratu kuti akubzala ufa.
(2) Umaganiza kuti ukabzala ufa ife sitidziwa.
20