Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 208
Paphata pa Chichewa
(b) Kutututsa gule ngati mmene amachitira Achewa.
Chitsanzo: Zikuoneka kuti zilombo zawedza.
Kuwenga:
(a) Kudwalitsa matenda enaake monga chipere.
Chitsanzo: Nsomba ya bombe imandiwenga.
(b) Kudula zikhadabo ndi lumo.
Chitsanzo: Amene sanawenge zala saadya ndi ine!
Kuwerengera mbewa ndi michira yomwe: Kuwerengera
zinthu zoti kulibe.
Chitsanzo: Kodi nafenso timangowerengera ndi michira
yomwe?
Kuwerengera: Kudalira pomwepo.
Chitsanzo: Nanenso ndikuwerengera pomwepa.
Kuweta ana: Kulela ana mowasasatitsa.
Chitsanzo: Kodi ana anuwa mumawaweta bwanji?
Kuweyeseka:
(a) Kutoperetu.
Chitsanzo: Koma ndiye ndaweyeseka ndi ulendowu.
(b) Kutheratu, kugwa.
Chitsanzo: Nyumba yawo yaweyeseka ndi mphepo.
Kuwezuka:
(a) Kuyamba kuphya.
Chitsanzo: Mango ayamba kuwezuka.
(b) Kusintha mtundu, kuyera.
Chitsanzo: Akumasamba kawirikawiri kuti awezuke.
(c) Kukhala woyera.
Chitsanzo: Ana awo onse ndi owezuka.
Kuwiringula: Kudandaula, kunyinyirika.
Chitsanzo: Anthu onse omwe ankawiringula
anawapirikitsa.
Kuwiringula: Kukana mlandu.
Chitsanzo: Atamufunsa ngati anali wolakwa, anayamba
kuwiringula.
207