Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 207
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: Akagula kanyama amafuna kumatiwalira
ndipo amatulutsa mbaula n’kumaphikira pabwalo.
(2) Kuoneka bwino.
Chitsanzo: Anzathu ndiye mukuwalatu!
Kuwapezerera: Kuwapeza akuchita zinthu zoipa
mwadzidzidzi.
Chitsanzo: Anawapezerera akuba ndiwo mumphika.
Kuwawasa: Kufika povuta kwambiri.
Chitsanzo: Kuntchitoku kwawawasa.
Kuwawitsa moyo (kukuwawa): Kukwiya kwambiri.
Chitsanzo: (1) Zimene mwachitazi zawawitsa moyo wanga.
(2) Mwachitazi zandiwawa.
Kuwayawaya: Kuyendayenda.
Chitsanzo: Akungowayawaya m’taunimu.
Kuwaza mchenga m’maso: Kupusitsa.
Chitsanzo: Akabwera, musalole kuti akuwazeni mchenga
m’maso.
Kuwaza:
(a) Kuchita zinthu zosangalatsa kapena kukhala
wosangalatsa kwambiri.
Chitsanzo: (1) Nkhani imene amafotokoza yandiwaza
kwabasi. (2) Amwene inuyo mumandiwaza kwambiri.
(b) Kuswa chipika ndi nkhwangwa kapena chinthu china.
Chitsanzo: Awaza nkhuni zambirimbiri.
Kuwedza:
(a) Kusinza. Nthawi zambiri munthu akamasinza
amagwetsa mutu, ndiye akadzidzimuka amaudzutsa.
Zimenezi n’zofanana ndi zimene zimachitika munthu
akamawedza.
Chitsanzo: Chifukwa cha kutentha, anthu ambiri
akumawedza.
206