Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 206
Paphata pa Chichewa
Kuvala ngati akupita kubafa: Kuvala zovala zosayenera
kuvala pagulu.
Chitsanzo: Kodi abambo amene aja amangoyayang’ana
akazi awo aja akumavala ngati akupita kubafa?
Kuvinidwa: Mawuwa anabwera kuchokera ku mwambo
umene umachitika m’zikhalidwe zambiri woti mwana
akakula amamupititsa ku chinamwali kuti akamuphunz-
itse zoyenera ndi zosayenera kuchita. Mwana aka-
malephera kusonyeza khalidwe labwino amangoti ndi
wosavinidwa.
Chitsanzo: N’chifukwa chiyani umachita mwano, kusav-
inidwa eti?
Kuvula munthu: Kukulalatira, kukutukwana.
Chitsanzo: Kaya ayambana nawo chiyani? Anawavula
anzawo palaini ngati pamene paja.
Kuvulalira mkati:
(a) Kutenga matenda opatsirana pogonana.
Chitsanzo: Mayiyu anavulalira mkati.
(b) Kumva kupweteka mumtima.
Chitsanzo: Sindikufuna kuonetsera, ndikungovulalira
mkati.
(c) Kuvulala mkati mwa thupi utachita ngozi.
Chitsanzo: Atachita ngoziyo anavulalira mkati moti
sipanatenge nthawi anamwalira.
Kuvulira kachipewa: Kupereka ulemu.
Chitsanzo: Mwayenda ulendo wonsewu wapansi?
Takuvulirani kachipewa.
Kuvundula: Kusokoneza, kupukusa.
Chitsanzo: Ndani amene wavundula madziwa.
Kuvunganyiza: Kusakanizasakaniza.
Chitsanzo: N’chifukwa chiyani wavunganyiza zovalazi?
Kuwala:
(a) Kuyerekedwa, kudzitama.
205