Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 205
Paphata pa Chichewa
Kuuma khosi: Kusamva.
Chitsanzo: Munthu wake ndi wouma khosi, kumulangiza
samamva.
Kuuma mtima: Kupanda chisoni.
Chitsanzo: (1) Andiumira mtima ndithu mpaka osan-
dipatsa. (2) Bambowa ndi wouma mtima.
Kuunguzaunguza:
(a) Kuganizaganiza.
Chitsanzo: Ataunguzaunguza, anaona kuti si bwino
kuyankha nthawi yomweyo.
(b) Kuyang’anayang’ana
Chitsanzo: Nditaunguzaunguza, sindinawaone.
Kuunikira: Kuthandiza munthu nzeru, kudziwitsa.
Chitsanzo: Sindinabwere kudzakuimbani mlandu,
ndimangofuna kukuunikirani.
Kuunjika: Kubiba, kunyera. Tanthauzo lake lenileni ndi
kuika zinthu zambiri pamalo amodzi.
Chitsanzo: Ndani waunjika m’chimangamu?
Kuupeza mtima: Osapupuluma, kumadekha.
Chitsanzo: (1) Achimwene, kumaupeza mtima, mudzapeza
zanu m’tsogolo. (2) Kuti upeze zabwino umafunika kuupe-
za mtima.
Kuusumana: Kumva bwino, kusangalala.
Chitsanzo: Ndinawapeza akuusumana pabala penapake.
Kuutha: Kudziwa kusewera mpira.
Chitsanzo: Mwanayu amautha mpira.
Kuutsa chenjerere: Kuchititsa kuti wina akwiye
kwambiri.
Chitsanzo: Mwana ameneyu wautsa chenjerere.
Kuutunga mowa: Kumwa kwambiri mowa, kuledzera.
Chitsanzo: Akautunga mowa amavuta kwambiri.
204