Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 204

Paphata pa Chichewa Kutula pansi: Kusiya udindo. Chitsanzo: Pulezidenti wadziko la Malawi watula pansi udindo wake. Kutumbiza: Kubereka mwana, mwana wina asanakule. Chitsanzo: Sindimafuna kudzatumbiza pamoyo wanga. Kutumbwa: Kuyerekedwa, kuchita matama. Chitsanzo: Anthu ena amayankhula motumbwa pamaliro ngati sadzafa. Kutupikana: Kutupa chifukwa cha matenda kapena kusowa zakudya m’thupi. Chitsanzo: Mwanayu akutupikana. Kutuwa: Kuvutika kwambiri. Chitsanzo: Chaka chino tituwa koopsa. Kutuzula maso: Kutulutsa diso lonse pamtunda. Chitsanzo: Akalusa amandiyang’ana atatuzula maso. Kuudziwa mpira: Kudziwa kusewera mpira. Chitsanzo: Mwanayu amaudziwa mpira. Kuugwira mtima: Kudziletsa kuti usayankhule kapena kuchita chinthu choipa. Chitsanzo: Achimwene anu aja amafunika munthu woug- wira mtima. Kuuluka (kutamba): Zokhudzana ndi ufiti. Mawuwa an- thu ena amawagwiritsa ntchito poganiza kuti munthu akhoza kuuluka usiku pogwiritsa ntchito tsache kapena lichero. Ndi zikhulupiriro chabe basi chifukwa palibe anaonapo zikuchitika. Chitsanzo: Nawonso anzanuwa akukhala ngati amauluka bwanji? Kuuluka: Kuthamanga kwambiri. Chitsanzo: Mwabwerako nthawi yomweyi, koma ndiye mwaulukatu! 203