Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 202

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Wodwalayo anayamba kutsalima ife tili pom- wepo. Kutsangula misozi: Kutonthoza ena, kupukuta misozi. Chitsanzo: Amene anabwera kudzatitsangula misozi ndi achimwene basi. Kutseguka m’maso: Kuzindikira. Chitsanzo: (1) Apatu ndiye mwanditsegula m’maso, sindi- madziwa kanthu. (2) Zimene a zaumoyo atiuza zatitsegula m’maso. Kutseguka m’mutu: Kuzindikira kapena kumvetsa zi- nazake. Chitsanzo: (1) Apatu ndiye ndatseguka m’mutu, sindi- madziwa kuti malambe ndi ofunika chonchi! (2) Ma- phunziro amenewa anditsegula m’mutu. Kutsegula pakamwa: Kuyankhula. Chitsanzo: Amaonekadi waulemu, koma akangotsegula pakamwa mpamene ndinadziwa kuti ndi khuluku. Kutsenjira: Kusowa osaonekanso, kuzimiririka, kubisika. Chitsanzo: (1) Anaima pakantinipo kwa nthawi yaitali, ko- ma kenako anangotsenjira. (2) Ndinyamuka dzuwa lika- tsenjira. Kutsika kwa mvula: Kugwa kwambiri kwa mvula. Chitsanzo: Koma ndiye chaka chino mvula yatsikatu. Kutsikira kulichete: Kumanda. Chitsanzo: Ana awo onse anatsikira kulichete. Kutsimphina: Kuyenda movutikira. Chitsanzo: Mwanayu watani akuyenda motsimphina? Kutsina khutu: Kuululira munthu chinsinsi. Chitsanzo: Ndinawakokera pambali kuti ndiwatsine khutu. Kutsinira mafulufute kuuna: Kutsekereza mwayi. Chitsanzo: Ukanalimbikira akanakupatsanso, koma watsinira mafulufute kuuna. 201