Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 197
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: (1) Mwana akatha msinkhu amayamba kuvuta.
(2) Mwana asanathe msinkhu mumafunika kumulangiza
kuti asadzadabwe thupi lake likayamba kusintha.
Kutha psiti: Kutheratu, kufa onse.
Chitsanzo: Atsikana onse othamanga anatha psiti.
Kutha thupi: Kuwonda.
Chitsanzo: Pamene mwanayu akukulamu wayamba kutha
thupi.
Kuthamanga magazi: Kupupuluma, kusaugwira mtima.
Chitsanzo: Mayi musathamange magazi, tikupatsani!
Kuthamanga mwazi: Kupupuluma, kusaugwira mtima.
Chitsanzo: Mayi musathamange mwazi, tikupatsani!
Kuthamangathamanga: Kugwira ntchito kapena kuchita
bizinezi kuti upeze kenakake.
Chitsanzo: Ndikapanda kuthamangathamanga ndidya chi-
yani m’tauni muno?
Kuthamangitsa:
(a) Kuuza munthu kuti achoke.
Chitsanzo: Ana awo aja anawathamangitsa pakhomo.
(b) Kuthamanga kuti ugwire munthu kapena kumupiri-
kitsa.
Chitsanzo: Akuthamangitsa galu.
Kuthamangitsa: Kuuza munthu kuti achoke pakhomo.
Angatanthauzenso kutsatira munthu amene akuthawa
pomuthamangitsa.
Chitsanzo: Anawathamangitsa palendi chifukwa sankali-
pira.
Kuthambitsa: Kukhaulitsa.
Chitsanzo: Amuthambitsa anzake odziwa zigogodo.
Kuthambitsa: Kukhaulitsa.
Chitsanzo: Manoma athambitsa Siliva ndi zigoli ziwiri kwa
du.
196