Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 196

Paphata pa Chichewa (c) Kumwa. Chitsanzo: Tiyeni tikatchaye tiyi. Kutchetcherera: Kukopa mkazi kapena mwamuna kuti ugone naye. Amayerekezera zimene tambala amachita ak- amafuna thadzi. Chitsanzo: Anyamatawa akumatchetcherera atsikana. Kutchukuma: Kuvutika kugwira ntchito kapena kugulitsa kanthu koma osapeza ndalama. Chitsanzo: Malonda avuta patauni pano, ukumatha kutchukuma tsiku lonse, osapeza olo 1 tambala. Kuteketa (tekedza): Kudya. Chitsanzo: Chichokere m’mawa akungoteketa makaka. Kutemberera: Kunenera zoipa kuti zidzamuchitikire. Chitsanzo: Umphawiwutu anakutembererani agogo anu! Kutenderera: Kukometsera. Chitsanzo: Nkhani yake ija anaitenderera kwambiri moti imangokhala ngati yabodza. Kutenga mtima: (a) Kukopa. Chitsanzo: Ndalama zija ndi zimene zinanditenga mtima. (b) Kupweteketsa mtima. Chitsanzo: Mawu ananena aja ananditenga mtima. Kutenga zosatenga: Kutenga matenda. Chitsanzo: Ndamva kuti ukuyenda ndi mtsikana wotakata uja, samala utenga zosatenga. Kutengeka: Kukopeka ndi chinthu. Chitsanzo: Mwanayu ndi wotengeka. Kutha mawu: Kuyankhula kwambiri, kulalata. Chitsanzo: Ukakhala walungalunga osamatha mawu, chilemba chimachita kubwera. Kutha msinkhu: Kukula, kuyamba kusamba kapena kutulutsa umuna. 195