Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 195

Paphata pa Chichewa Kutasa: Kuchita zinthu moyerekedwa, kuchita zinthu momasuka kwambiri, kukomedwa. Chitsanzo: Mmene achokamu mpamene wantchito uja watasa. Kutaya bomwetamweta: Kutaya mwayi wopezapeza. Chitsanzo: Munakana zoona! Apa ndiye mwataya bomwe- tamweta. Kutaya madzi: Kukodza. Chitsanzo: Ndidikireni nditayeko madzi paselipa. Kutaya mimba: Kupha mwana wosabadwa. Chitsanzo: Boma likulola azimayi omwe atenga mimba zosakonzekera kuti azitaya mimba. Kutaya mtima: Kuyamba kuona kuti zinthu sizingayen- denso, sizingasinthe. Chitsanzo: Ndinataya mtima nditaona kuti zaka zikudutsa asakuimba foni. Kutaya nthawi: Kuononga nthawi. Chitsanzo: Mukungotaya nthawi yanu kulimbana ndi ine. Kutayira kamtengo: Kupereka ulemu. Chitsanzo: Ndawataira kamtengo, akanakhala ena sa- kanaugwira mtima! Kutchalitchi: Mawu amene amanenedwa ponena za kusukulu, popeza masukulu ambiri akale anali a tchalitchi. Chitsanzo: Ifetu kutchalitchi sitinapiteko, moti sitidziwa kuwerenga. Kutchatchatuka: Kuchenjeretsa. Chitsanzo: Mwana ameneyu ndi otchatchatuka. Kutchaya: Kumenya. (a) Chitsanzo: Mtsikana ameneyu ndimutchaya. (b) Kuimba, kukoka chingwe. Chitsanzo: Tiwatchayire lamya. 194