Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 194

Paphata pa Chichewa Kusweka mutu: Kukhala wolongolola, wovuta. Chitsanzo: Ntchito ngati zimenezi zimafuna anthu osweka mitu. Kutafula: Kulalata. Chitsanzo: Akayamba kutafula mungochokapo. Kutafuna mlandu: Kuyankhula pamlandu. Chitsanzo: Anthuwo atasonkhana, amfumu anayamba kuutafuna mlanduwo. Kutakataka: Kugwira ntchito, kuchita khama. Chitsanzo: Mkazi amafunika azikhala wotakataka. Kutalitali: Kulephereratu. Anganenedwenso potanthauza kuti si zoona ngakhale pang’ono. Chitsanzo: Kodi anapezadi zimene ankafuna? Kutalitali! Kutama (kutamanda): Kulemekeza. Chitsanzo: Ndi omwewo amene amakutamani, ine ayi. (2) Akuona ngati ndidziwatamanda! Kutambalala: (a) Kukhazikika. Chitsanzo: Musabweretu kudzatambalala pakhomo pano. (b) Kukhala moongola miyendo. Chitsanzo: Uli tambalale apa, m’malo moti uzikagwira ntchito uko! (2) Mwamuna sakhala motambalala. Kutamidwa: Kulemekezedwa. Chitsanzo: Amakutamani ndi akazi anu omwe aja, ine ayi! Kutantha: Kunena zina. Chitsanzo: Fotokoza bwinobwino iwe, osamangotantha. Kutapa m’kamwa: Kubwera kudzakufunsa kapena kud- zayankhula nawe kuti akutole zifukwa. Chitsanzo: Anabwera kuno kudzanditapa m’kamwa. Kutapakutaya: Zambirimbiri. Chitsanzo: Ndalama ife ndi kutapakutaya. 193