Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 192

Paphata pa Chichewa Kusowa mtengo wogwira: Kusowa chochita. Chitsanzo: Si bwino kumasekana pamavuto chifukwa na- wenso pamawa, ukhoza kudzasowa mtengo wogwira. Kusudzula: Kuuza munthu kuti azipita kwawo banja likatha. Nthawi zina anthu amawapatsa ndalama mwina 2 kwacha monga malipiro achipongwe osonyeza kuti awasudzula. Chitsanzo: (1) Pano sali pabanja, anawasudzula akazi awo. (2) Ingondisudzulani ngati simukundifuna, mwamuna si inu nokha padzikoli! Kusula: (a) Kufunira munthu mankhwala obereketsa. Chitsanzo: Ataona kuti zavuta, anapita kukasulitsa mankhwala. (b) Kuthandiza kuti ukhale wanzeru. Chitsanzo: Aphunzitsi a m’Malawi muno amasula ana okalowa m’sukulu za ukachenjede. Koma iwowo sasintha- yi. Amadzamwalira akukongolabe katapira. (c) Kupanga khasu kapena nkhwangwa. Zinthu zimene zimasulidwa zimakhala zachitsulo. Chitsanzo: Bambo anga amasula makasu. Kusunga chakukhosi: Kusunga chifukwa, kudana ndi munthu chifukwa cha zimene anakuchitira. Chitsanzo: Anthu amasangalala m’banja akamapanda kusungirana chakukhosi. Kusunga nthawi: Kubwera pa nthawi yake, kusachedwa. Chitsanzo: (1) Mabwana a pano sasunga nthawi. (2) Ali- yense azolowere kumasunga nthawi. Kusunsunuka: Kukula. Chitsanzo: Mwanayutu wasunsunuka, mpofunika mumu- patse malangizo. Kusupa (kufupa): Kupereka mphoto. Chitsanzo: Sindingasupe gule wosavinga bwino ngati ameneyu! 191