Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 191

Paphata pa Chichewa Kusoloka: Kutheratu kwa nyama kapena zomera. Chitsanzo: Mitundu yambiri ya nsomba inasoloka. Kusololoka: (1) Kukula mofulumira, kutalika. Chitsanzo Ana a masiku ano akumangosololokera m’mwamba. (2) Koma ndiye wasololokatu, mpaka kundi- posa msinkhu? Kusomeka: (a) Kuika munthu malo ena, kaya paudindo. Chitsanzo: Boma linadzatisomeka kumudzi kuno. (b) Kuzika mtengo kapena chinthu penapake. Chitsanzo: Someka mtengowu kutsindwiko. Kusongola: (a) Kudula chinthu kuti chisongoke, chikhale chobaya, mwachitsanzo kusongola pensulo. Chitsanzo: Akazi ambiri ali ndi milomo yokhala ngati achita kusongola. (b) Kukhala m’galimoto koma n’kutulutsa chigongono panja. Chitsanzo: Anzanu mkono wawo unapita chifukwa chokonda kusongola akakwera galimoto. (c) Kukhala pansi mosonyeza kuti ukumva bwino. Chitsanzo: Ndinakuonani mutasongola panjinga. Kusonkhezera: Kulimbiktsa. Chitsanzo: (1) Kumene mukuchitakutu ndi kusonkhezera mavuto! (2) Si bwino kumasonkhezera kuti anzako amenyane. Kusosa: Kudumpha tsiku limodzi. Nthawi zina amatan- thauzanso kuchotsa ntchire m’munda pokonzekera ku- limanso mbewu zina. Chitsanzo: Tingososa mawali, tidzapita mkucha. Kusosoka mthenga: kupusa. Chitsanzo: Munthu woyerekedwa amafunika kumusosola mthenga. 190