Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 19
Paphata pa Chichewa
Bongobongo: Ubongo.
Chitsanzo: Amachita zinthu ngati alibe bongobongo.
Bongwe: Mwana wasukulu yemwe wangobwera kumene
makamaka amene ali makalasi oyambirira. M’buyomo
anthu amenewa ndi amene ankazunzidwa akafika
pasukulu. Mawuwa angatanthauzenso munthu
wosadziwa zinthu.
Chitsanzo: Nafenso tinazunzika chonchi tili mabongwe.
Bopha: Kuvala.
Chitsanzo: Wabopha suti.
Bowa bwanga: Kuchedwa, kuchita zinthu mwachidodo.
Chitsanzo: Osamachita za ubowa bwanga.
Bububu: Munthu wosayankhula.
Chitsanzo: Akungokhala ngati bububu.
Bulutu: Munthu wopusa.
Chitsanzo: Mnzanu uja ndi bulutu.
Buluzi: Wopanda ntchito, wopanda nzeru.
Chitsanzo: Ndiwe buluzi eti!
Buma maliro: Kulira koyambirira pamaliro.
Chitsanzo: Tabwera titamva kubuma.
Bunobuno: Ali wosavala.
Chitsanzo: Wamisala uja akumayenda ali bunobuno.
Bunobwamuswe: Ali wosavala.
Chitsanzo: (1) Mmene anthu akuvalira masiku ano
n’chimodzimodzi kuyenda bunobwamuswe. (2)
Akumazungulira nyumba ali bunobwamuswe.
Buntha pakamwa: Kulephera kuyankhula bwino.
Chitsanzo: Mose anali munthu wobuntha pakamwa.
18