Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 188

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Atsikana ambiri amene amapita kuchinamwali, amachita mwambo wa kusasa fumbi. Kusasa: Kukana munthu, kusiya kucheza naye. Chitsanzo: Kodi anzanu aja anakusasani? Kusasantha: kumenya modetsa nkhawa. Chitsanzo: Akakugwiratu akusasantha. Kusasatuka: Kutengeka kwambiri. Chitsanzo: Ndani angafunsire mtsikana wosasatuka ngati ameneyu! Kusatha phazi: Kusasiya kupita kwinakwake. Chitsanzo: Satha phazi pakhomo pano. Kusationa tulo: Kusagona. Chitsanzo: Dzulo sindinatione tulo, ndimamva kutentha ngati ndili m’bokosi. Kusavuka: Kuonekera poyera, kupusa. Chitsanzo: Khalidwe lanuli musavuka nalo! Kusefukira: (a) Kudzadza kwambiri kwa madzi. Chitsanzo: Katundu wawo anapita ndi madzi osefukira. (b) Kuyankhula mosaganiza bwino. Chitsanzo: Nthawi zambiri amayankhula mosefukira. (c) Kutayikira. Chitsanzo: Thobwa likusefukira m’kapu. Kuseka chikhakhali (chikhakhade): Kuseka kwambiri. Chitsanzo: Ukayankhula zopanda mnzeru amakuseka chikhakhali. Kusekana zikundu: Kunyozana mavuto omwe nonse muli nawo. Chitsanzo: Tisamasekane zikundu eti! Musaiwaletu kuti nanunso khalidwe lanu ndi lomweli. Kusekana zikundu: Kuseka mavuto omwe nonse muli nawo. Chitsanzo: Tonse ndi akuda ngati makala, ndiye 187