Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 186
Paphata pa Chichewa
Kusalowa m’nyumba: Kusagonana ndi mkazi kapena
mwamuna wako.
Chitsanzo: Akazi awo amadandaula kuti amuna awo
salowa m’nyumba pomwe amagona momwemo.
Kusamba zitsulo: Mawu amenewa amanenedwa ngati
munthu wachedwa kwambiri kubafa. Pokokomeza
amanena kuti wachedwa chifukwa m’malo mosamba
madzi, amasamba zitsulo.
Chitsanzo: Kodi kubafako mukusamba zitsulo?
Kusamba:
(a) Munthu amene ali nazo zambiri ndipo zina aman-
goseweretsa.
Chitsanzo: Anzathutu mukusamba m’ndalama!
(b) Matenda amene azimayi amadwala mwezi ndi mwezi.
Chitsanzo: Mtsikana akamangolusa popanda chifukwa,
amakhala kuti akusamba.
Kusambira m’manja:
(a) Kugwira ntchito mwaluso zedi.
Chitsanzo: Nyumbayo anaimanga moisambira m’manja.
(b) Kuchita zinazake kuti pamapeto pake usadzakhale ndi
mlandu, kunyanyalira.
Chitsanzo: Katundu wanu ndi uyu, zikakuvutani mu-
sabwere, ndakusambirani m’manja.
Kusambira m’ndalama: Kukhala ndi ndalama zochuluka
kwambiri.
Chitsanzo: Azibusa ambiri akusambira m’ndalama chifu-
kwa chochita bizinezi yoopseza anthu ndi Gehena.
Kusambitsa ndi zibakera: Kumumenya koopsa.
Chitsanzo: Mwanayo anawasambitsa bambo ake ndi
zibakera.
Kusambuka: Kunyozeka, kuvutika.
Chitsanzo: (1) Akutinyoza chifukwa tasambuka. (2)
Anzanu aja andisambula.
185