Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Página 184
Paphata pa Chichewa
(b) Kusaphedwa kapena kusakumana ndi tsoka linalake.
Chitsanzo: Anapulumuka pa ngozi yoopsa.
(c) Kuchitika mwangozi kapena mwadzidzidzi.
Chitsanzo: Chiphwisi chinandipulumuka.
Kupumuntha: Kumenya munthu mwankhanza.
Chitsanzo: Akakupeza ukuchita zimenezo akupumuntha.
Kupunduka: Kukhala ndi chilema.
Chitsanzo: Ali ndi ana awiri opunduka.
Kupungula mpweya: Mawu amene eni nyumba amauza
mlendo akamafuna kumuuza kuti anene chimene wabw-
erera.
Chitsanzo: Tati tikupunguleni mpweya!
Kupunthwa: Kulakwitsa chinachake.
Chitsanzo: Munthu aliyense amapunthwa nthawi zina.
Kuputa mavuto: Kuyamba dala zinthu zomwe zikhoza
kukuika m’mavuto.
Chitsanzo: (1) Anawa andiputira mavuto. (2) Amenewatu
akuwaputa mavuto, aziona!
Kupuwala: Kukhala ndi chilema.
Chitsanzo: Amalume awo ndi opuwala.
Kupwaira: Kugwira mwankhanza.
Chitsanzo: Atsamunda anapwaira anthu onse omwe
ankalimbana nawo.
Kupwintha: Kuika zambiri, kuwonjezeza zambiri.
Chitsanzo: (1) Mu ndiwozi apwinthamo mchere wambiri.
(2) N’chifukwa chiyani mwapwintha ufa wambiri chonchi?
Kupyolera: Kudzera.
Chitsanzo: Amatumiza zinthu kupyolera pabasi.
Kupyontha: Kumwa, kuyamba, kutsopa.
Chitsanzo: Ndinawapeza akupyontha kabotolo ka mame.
183