Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 178
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: M’munda analima chimanga muja aphinziramo
mbatata.
Kuphipha: Kugwedezekagwedezeka kapena kuti kuthatha
komwe kumachitika munthu kapena nyama zina zikatsa-
la pang’ono kufa kapenanso zikapanikizika.
Chitsanzo: (1) Nsombayo inayamba kuphipha ataiponyera
pamtunda. (2) Aliyense anayamba kulira munthuyo
atayamba kuphipha.
Kuphofomoka: Kugwa modetsa nkhawa.
Chitsanzo: Mwana wanu waphofomoka mumtengo.
Kuphotchora: Kusiya mkazi kapena mwamuna wako
n’kukagona ndi wina.
Chitsanzo: Mwamunayu anaphotchora.
Kuphuka: Kuchira.
Chitsanzo: Achibale onse omwe amafuna kulanda chuma,
sanasangalale ataona kuti m’bale wawo waphuka.
Kuphula:
(a) Kuchiritsa munthu nthenda imene yakanika
asing’anga ena.
Chitsanzo: Amene uja amadwala mwakayakaya, kaya ndi
ndani wamuphula?
(b) Kulemera, kupeza ndalama zambiri.
Chitsanzo: Anthu onse omwe ndinayamba nawo bizinezi
anaphula.
Kuphuluza: Kulakwitsa, kusaponda kapena kugwira
bwino.
Chitsanzo: Anamuchotsa ntchito ataphuluza n’kuyamba-
na ndi abwana.
Kuphuluza: Kuteleleka, kulakwitsa, kuponda kapena
kugwira molakwika.
Chitsanzo: Ndinaphuluza n’kubinya phazi.
Kuphupha: Kudzimenyetsamenyetsa.
Chitsanzo: Khukuyo ataidula mutu inayamba kuphupha.
177