Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 177

Paphata pa Chichewa Kupheduka: Kuululika. Chitsanzo: (1) Muyaluka nkhaniyi ikapheduka. (2) Ndani amene waphedula nkhaniyi? Kuphera mphongo: Kutsirira ndemanga, kusonyeza kuti ukugwirizana ndi zimene wina wanena. Chitsanzo: Ndikufuna kuphera mphongo pa mawu amene akuluwo anena. Kuphera ufulu: Kulakwira munthu posalemekeza ufulu wake. Chitsanzo: Ana a masiku ano ukamawauza kuti asamava- le ngati akupita kubafa, akumakuyankha kutu usawaphere ufulu. Kuphetsa: (a) Kugulitsa. Chitsanzo: Ndaphetsa njinga yanga ija. (b) Kupweteketsa munthu wina, kuchititsa kuti wina aphedwe. Chitsanzo: Zimene mukuchitazi muwaphetsatu akazi anu aja. Kuphikana (kuphika): Kumenyana, kumenya munthu. Chitsanzo: (1) Ndinawapeza akuphikana. (2) Anzake amuphika. Kuphikitsa thobwa: M’madera a m’chigawo chapakati, amati akaphika thobwa, amadzaliwiritsanso kachiwiri. Zimene amachitazi amati kuphikitsa thobwa. Chitsanzo: Kodi mwaphikitsa thobwali? Kuphimba m’maso: Kupusitsa, kunamiza, kunyenga. Chitsanzo: Akungofuna kutiphimba m’maso. Kuphinza: Kuvala. Chitanzo: Koma ndiye waphinza kasuti kabwinotu! Kuphinzira mbatata: Kulimba mtumbira n’kudzalapo mbatata. 176