Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 172

Paphata pa Chichewa Kuona m’magonero: Kudziwa mmene ulili. Chitsanzo: Osamangoitana aliyense kuti abwere kwanu angadzakuone m’magonero n’kukubera. Kuona m’mimba: Kuyang’ana mwamwano. Chitsanzo: Musandiyang’ane ngati mukundiona m’mimba. Kuona manthu wamavuto: Kukumana ndi mavuto aaku- lu kwambiri, mavuto osaneneka. Chitsanzo: Chaka chino ndiona manthu wamavuto. Kuona ndi diso limodzi: Nyoza. Chitsanzo: Anzake amangowaona ndi diso limodzi. Kuona ng’ala: Kusaona bwino. Chitsanzo: Munaona ng’ala, si mango ndi mapapaya. Kuona ngati wavula: Kukuyang’ana monyoza kapena kukuona ngati munthu wopusa. Chitsanzo: Anzakefe amangotiona ngati tavula. Kuona patali: Kuganizira zotsatira za zimene ukuchita kapena kuganizira za m’tsogolo. Chitsanzo: Pulezidentiyu amaona patali. Kuona zilubwelubwe: Kusokonezeka, kuona zinthu zosi- yana kwambiri ndi zimene zilipo. Chitsanzo: Nanunso mwayamba kuona zilubwelubwe. Kuoneka bo: Mawu amene achinyamata amanena poyamikira munthu kuti akuoneka bwino. Chitsanzo: Msungwana, ukuoneka bo! Kuoneka ngati kamvuluvulu: Kuvala zovala zosaoneka bwino, kuvala nsanza. Chitsanzo: Kutchena konsekuja, makolo awo amangoon- eka ngati kamvuluvulu! 171