Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 17

Paphata pa Chichewa Bibida: Mowa. Chitsanzo: Bibida ndi amene amawalowa m’thumba, moti akapeza ndalama pakhomo pano pamawayabwa. Bingiza: Chimpopamanyi. Chitsanzo: Akufuna aitanitse chibingiza. Birimankhwe (tonkhwetonkwe): Munthu wosinthasitha. Chitsanzo: Amene uja ndi birimankhwe (tonkhwetonkhwe). Akangochoka kutchalitchi amavula Chikhirisitu n’kuchisiya apo, kenako amavala usatana. Biriwira: Kukhala ndi thanzi, kunenepa. Chitsanzo: Chaka chino tibiriwira, chakudya ndi kutapa kutaya. Bisa nkhope: Kukhala ngati sukuona. Chitsanzo: Osamabisa nkhope ukakumana ndi wachibale. Bisala pachipande: Kunama Chitsanzo: Ameneyu akubisala pachipande. Bisira kampeni kumphasa: Kuchitira munthu chiwembu. Chitsanzo: Ndimadziwa kuti amandibisira kampeni kumphasa. Bizinezi yotentha: Bizinezi yobweretsa ndalama zambiri. Chitsanzo: Akuchita bizinezi yotentha. Bobobo: Kuchedwachedwa, chidodo. Mawuwa anachokera pa kankhani kena konena za munthu wachibwibwi yemwe anapita ndi anzake kukazula bowa. Ndiye mukamayenda gulu, munthu amene wayambirira kuona bowa amafunika kunena mokweza kuti “bowa wanga!” kuti anzake adziwe kuti wayambirira kuona bowayo ndi iyeyo. Ndiye wachibwibwi uja ankangoti bo bo bo, osamalizitsa. Nthawi 16