Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 168

Paphata pa Chichewa Kunkhuniza: Kuyankhula mobisa. Chitsanzo: Mnyamata amene uja wandikunkhuniza. Kunola mano: Kukonzekera kudya zankhuli. Chitsanzo: Mpofunika tinole mano, tidyera nyama lero. Kunong’a: Kukoma. Chitsanzo: Kekeyu ndiye akunong’atu! Kunong’oneza bondo: Kudzimvera chisoni kapena kud- ziimba mlandu chifukwa cha zimene unasankha mo- lakwika. Chitsanzo: Anthu onse omwe sankalimbikira sukulu amanong’oneza bondo. Kunsakhuta: Kumanda. Chitsanzo: Mbava ija tinakaikwirira kunsakhuta. Kunsitu: Kumanda. Chitsanzo: Masiku ano mitengo yatsala kunsitu kokha. Kunyalanyaza: Kusafuna kuganizira zoipa zimene wina wakuchitira, kusafuna kuchita zinazake. Chitsanzo: (1) Anandilakwira koma ndinangosankha kuinyalanyaza nkhaniyo. (2) Munthu ameneyu amakonda kunyalanyaza pochita zinthu. Kunyangala: Kuvuta, kuipa, kulusa. Chitsanzo: (1) Agalu ake ndi onyangala. (2) Akazi awo aja ndi wonyangala. Kunyanyala: Kukwiya, kusiya kuchita zinazake. Chitsanzo: Anyanyala chifukwa choti tawakaniza njinga. Kunyanyula: Kuputa munthu, kuchititsa kuti munthu akwiye. 167