Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 165
Paphata pa Chichewa
Kumwaza ndalama: Kugwiritsa ntchito ndalama
mosasamala.
Chitsanzo: Amuna anu achoka osasiya ndalama yandiwo
aja akumwaza ndalama m’taunimu.
Kumwera madzi:
(a) Kugulitsa.
Chitsanzo: Anali ndi nyumba koma anaimwera madzi.
(b) Kuzisiya, kusaganizira kwambiri nkhani inayake.
Chitsanzo: Nkhani ija ndangoimwera madzi, sindikufuna
zoyambana nawo.
Kumwera:
(a) Kugwiritsa ntchito ndalama pogula mowa.
Chitsanzo: Salale yonse wamwera.
(b) Kumvetsa zinazake, kudziwa kwambiri zinazake.
Chitsanzo: Masamuwa ndiye ndamwera, atabwera pa-
mayeso sindingalephere.
Kumwera:
(a) Kumwa madzi utadya chakudya.
Chitsanzo: Ndakhuta, tsopano ndimwere madzi.
(b) Kudziwa zinthu, kuloweza zinthu.
Chitsanzo: (1) Masamu amenewa ndinamwera. (2)
Phunziro limeneli ndalimwera.
Kundade: Munthu woyendayenda.
Chitsanzo: Ukakhala kundade, zambiri zimakuphonya.
Kundipatsa maganizo: Nkhani kapena chinthu chimene
chingachititse kuti uziganiza kwambiri.
Chitsanzo: Mwana ameneyu amandipatsa maganizo.
164