Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 164

Paphata pa Chichewa Kumushisha: Kumuopseza. Chitsanzo: Kunabwera anyamata enaake ndipo anayamba kumushisha. Kumutembenukira: Kumuukira, kusiya kugwirizana naye. Chitsanzo: Amene uja tsiku lina adzakutembenukirani. Kumuwaza mchenga m’maso: Kumupusitsa. Chitsanzo: Anachenjera anzake atamuwaza mchenga m’maso. Kumva bwino: Kusangalala. Angatanthauzenso kumva kukoma. Chitsanzo: Amamva bwino anzake akamavutika. Kumva m’bebe: (a) Kukhaulitsa. Chitsanzo: Mumawanyoza asanabwere, ndiyetu mumva m’bebe chifukwa akuchitani zoopsa. (2) Kumva kutentha. Chitsanzo: Ndiyandikireko motowu kuti ndizimva m’bebe. Kumva mwala kupuma: Dziwa kuti pali kanthu kabwino. Chitsanzo: Kodi galuyu akununkhidza pamenepa chifukwa chiyani? Wamva mwala kupuma! Kumvera m’maso: Kusamva. Chitsanzo: Ndinakuuzanitu posachedwapa, kodi nanunso mumamvera m’maso? Kumwa inki: Kuphunzira. Chitsanzo: Anthu amene anamwa inki savutikiratu. Kumwaza maso: Kuyang’ana uku ndi uku. Chitsanzo: Nditamwaza maso sindinawaone. 163