Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 163

Paphata pa Chichewa Kumtima kwalira nkhwichi: Kuvutika mumtima. Chitsanzo: Bwanayo anazindikira kuti kwabwera munthu wina wamapepala abwino kuposa ake, kumtima kunalira nkhwichi. Kumtima mbee ngati waponda muufa: Kumva bwino kwambiri utachita chinachake. Chitsanzo: Kumtima kwake kuli mbee ngati waponda muufa. Kumudwala: Kufunitsitsa kuona munthu winawake. Chitsanzo: (1) Mayi anga ndawadwala. (2) Ndabwera chifukwa ndinakudwalani. Kumudzala: Kulola munthu kukhazikika, kumunyen- gerera. Chitsanzo: Koma ndiye mukumudzalatu, abweranso mawa muona! Kumukonda mpaka aiwale kwawo: Kumukonda kwam- biri kuti asalakelakenso zobwerera kwawo. Chitsanzo: Uzimukonda kwambiri kuti aiwale kwawo. Kumukuntha nayo ndodo (kumuphimba nayo ndodo): Kumukwapula, kumumenya. Chitsanzo: Mnzanu anabwera mochedwa uja amuphimba nayo ndodo. Kumumvetsa madzi: Kumukhaulitsa. Chitsanzo: Amayerekedwa ndiye anzake anamumvetsa madzi. Kumupukwa: Kufunitsitsa kuona munthu winawake. Chitsanzo: Makolo anga ndawapukwa. 162