Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 159
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: Anapunthwa moti anangotsala pang’ono
kuluma pansi.
Kulumana: Kukangana, kuyambana.
Chitsanzo: (1) Ndinawapeza akulumana. (2) Akakhala ma-
lo amodzi sachedwa kuyamba kulumana. (3) Anyamata
okondana aja alumana.
Kuluwika: Kulankhula mawu omwe anthu ena
sangawamve msanga.
Chitsanzo: Pamenepatu ndiye mwandikuluwika, kuwoloka
moto n’kutani?
Kum’thyapa: Kum’menya.
Chitsanzo: (1) Ukapitiriza kuvuta ndikuthyapa! (2) Mwa-
nayu ndi wofunika kum’thyapa.
Kumaiwerenga: Kumayamba waganiza kaye.
Chitsanzo: Usanayambe chibwenzi umafunika kuma-
yamba waiwerenga kaye.
Kumalikukutu: Kumanda.
Chitsanzo: Masiku ano mitengo yatsala kumalikukutu
kokha.
Kumanga m’masamba: Kubisira munthu zinazake,
kupusitsa, kunamiza.
Chitsanzo: Anzanuwotu akumangani m’masamba.
Kumangika: Kusamasuka, kunjatika, kuchita zinthu
mwamantha.
Chitsanzo: Musamangike, mukhoza kudya zimene
mukufuna.
Kumangira mpanda: Kuletsa kuyendayenda.
Chitsanzo: Akachoka pano akumakaonana ndi anyamata.
158