Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 157

Paphata pa Chichewa Kulowa m’manda: Kuikidwa m’manda, kumwalira. Chitsanzo: Akazi awo analowa m’manda chaka chatha. Kulowa m’maso: Kusowa choti ungatenge. Chitsanzo: Ndikulephera kusankha chabwino, zandilowa m’maso. Kulowa m’mimba: Kukuopseza. Chitsanzo: Akuchita zimenezi kuti angondilowa m’mimba. Kulowa m’nthumba: Kuwononga ndalama. Chitsanzo: Nyumba ija ndi imene yawalowa m’nthumba. Kulowa m’nyumba: Kugonana. Chitsanzo: Banja lawo linatha chifukwa mwamuna sankalowa m’nyumba. Kulowa mphepo: Kuyamba kuvutavuta, kusokonekera. Chitsanzo: (1) Banja lawo lalowa mphepo. (2) Mukayamba mwano mulowetsa mphepo m’banja mwanu. Kulowa mphepo: Kuyamba kuvutavuta. Chitsanzo: Tekinoloje ikupangitsa kuti mabanja ambiri alowe mphepo. Kulowa mphuchi: Kulowa matenda. Chitsanzo: Moyo wathu wangolowa mphuchi. Kulowa pansi: Kusayenda bwino kwa bizinezi kapena zinthu zina. Mawuwa angagwiritsidwenso ntchito ponena za kuchepa kwa makhalidwe abwino. Chitsanzo: (1) Makhalidwe abwino akulowa pansi. (2) Bizinezi yake ikulowa pansi. (3) Bizinezi yawo itayamba kulowa pansi, m’golosale yawo munangotsala zinthu zo- sadyedwa zokhazokha monga malezala, mabatani ndi masingano. 156