Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 152

Paphata pa Chichewa Kulembeka pachipumi: Kuonekera kwa onse. Chitsanzo: (1) Nkwiyo wawo unalembeka pachipumi. (2) Si bwino kumalola kuti umphawi wako uchite kulembeka pa- chipumi. Kulenga: Kuchepa. Chitsanzo: Mwana amene uja akulenga, sangalimbane ndi ine. Kulera: (a) Kusamalira. Chitsanzo: (1) Mkazi amene uja adzamulera. (2) Makolowa amadziwa kulera ana. (b) Kutsata njira zothandiza kuti musabereke mwana. Chitsanzo: Anayamba kulera kuti asamangotumbiza ana. (c) Kukhwefuka. Chitsanzo: Chingwechi chalera, mpofunika tichikungenso. Kulerera pachilolo: Kulera monyengerera, kusasatitsid- wa. Chitsanzo: Mwanayu ndi wopusa chifukwa anamulerera pachilolo. Kulerera pachinena: Kulera mwana momunyengerera, kusalera bwino mwana. Chitsanzo: Ana awo aja amawalerera pachinena. Kulewa: Kuzemba, kuzinda. Chitsanzo: Akanapanda kulewa chibakeracho akanamugulura mano. Kuleza mtima: Kudekha, kudikira, kuchedwa kupsa mti- ma. Chitsanzo: Kuyendetsa galimoto kumafuna munthu wole- za mtima. 151