Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 151
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: Mtengwayu wayamba kuulavulatu mwano,
mpaka kufika ponena kuti anabwerera banja osati ukapo-
lo?
Kulavulira khala lamoto: Kulalatira wina utakwiya
kwambiri.
Chitsanzo: Tiyeni tichokepo. Mmene akuyang’aniramo
akhoza kutilavulira khala la moto.
Kulawa zamchere: Kuchita zinazake zomwe sungafunen-
so kuzisiya.
Chitsanzo: Ndinadziwa kuti akadzangolawa zamchere
sadzafunanso kusiya.
Kulawa:
(a) Kungoyamba pang’ono.
Chitsanzo: Filimuyo sitinaionere mpaka kuimaliza. Anan-
gotilawitsako pang’ono.
(b) Kumwa mowa.
Chitsanzo: Amakonda kuyankhula chingelezi akalawa.
Kulefuka: Kufooka.
Chitsanzo: (1) Zimene andiuza zandilefula. (2) Ndangolefu-
kiratu!
Kulekana: Kusiyana.
Chitsanzo: Mavutowa ndilekane nawo.
Kulekerera mwana: Kulera mwana momunyengerera,
kusalera bwino mwana.
Chitsanzo: Makolo anu anakulekererani, n’chifukwa chake
munakula mopusa chonchi.
Kulema: Kutopa.
Chitsanzo: Analema ndi mavuto.
150