Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 149
Paphata pa Chichewa
Kukusowa: Kufunitsitsa utaonana ndi munthu winawake.
Chitsanzo: Wachikondi wanga ndamusowa.
Kukutembenukira: Kusintha poyerayera, kukuukira.
Chitsanzo: Tinagwirizana bwinobwino koma titafika
ananditembenukira.
Kukutumula: Kumenya koopsa, kusansa.
Chitsanzo: (1) Akukutumulanitu! (2) Takutumulani mpha-
sayo!
Kukuyabwa: Kusakusangalatsa, kukukwana.
Chitsanzo: Chizolowezi chanuchi chimandiyabwa.
Kukuzolowera: Kusiya kukulemekeza.
Chitsanzo: (1) Musandizolowere choncho, lero ndiku-
masulani! (2) Ana amenewa ayamba kundizolowera.
Kukwangula m’kamwa: Kudyera nyama.
Chitsanzo: (1) Lero m’kamwa mwathu mwakwangukako.
(2) Lero tiphe nkhuku kuti tikwanguleko m’kamwa.
Kukwapatira: Kuika chinthu munkhwapa, kupana chin-
thu ndi nkhwapa kuti chisagwe.
Chitsanzo: Akwapatira kachikwama.
Kukwatira chiwiri: Kukhala ndi akazi awiri, mitala.
Chitsanzo: Bambowa anakwatira chiwiri.
Kukwatiwa mwamlato: Kukwatiwa kapena kuchita
chinachake mtima uli kwina.
Chitsanzo: Anangokwatira mwamlato, mkazi uja
samufuna.
Kukwawa kukaona abale: Kuyendera achibale, kupita
malo ena.
Chitsanzo: (1) Ndikufuna ndikwawire kumudziku kuti
148