Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 148

Paphata pa Chichewa Kukumaliza: Kukusangalatsa. Chitsanzo: Nyimboyi imandimaliza. Kukumana nazo: Kukumana ndi mavuto. Chitsanzo: Akapitiriza utambwali akumana nazo. Kukunkha: Kutolera zinthu zotsalira. Chitsanzo: Ndikupita kukakunkha m’munda wa agogo. Kukunthumula: Kumenya. Chitsanzo: Amukunthumula anzake. Kukupanga kanyenya: Kukupweteka. Chitsanzo: Usamale nawo anthu amene aja ndi zi- gawenga. Akhoza kukupanga kanyenya. Kukuphonya: Kusakumana nazo, kusemphana nazo. Chitsanzo: Nkhani imeneyi inandiphonya. Kukuponya miyala: Kukutaya, kusiya kukuthandiza. Chitsanzo: Ayamba kutiponya miyala chifukwa choti ta- sauka. Kukupula: (a) Kumenya. Chitsanzo: Awakupula anzawo. (b) Kuwaula khungu. Chitsanzo: Anapsa ndi madzi otentha moti khungu lake lakupuka. Kukusa: Kuchititsa munthu kuti abwere kapena apita malo enaake. Chitsanzo: Ntchito ndi zimene zikukusa anthu kuti abwere m’tauni muno. Kukusira pamodzi: Sonkhanitsa, ika pamodzi. Chitsanzo: Anthu onse ochedwa awakusira pamodzi. 147