Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 147
Paphata pa Chichewa
chifukwa apolisi anali pomwepo. (2) Ndinawaona
akumukukutira mano.
Kukukwana: Kutopa nazo, kusasangalala ndi chinthu.
Chitsanzo: (1) Nkhani imeneyi yandikwana. (2) Khalidwe
lanuli landikwana.
Kukula chiwindi: Kuchita makani.
Chitsanzo: M’gowelo muno sitifuna mwana wokula
chiwindi.
Kukula mopulukira: Kukula mopusa, kusakula ndi kha-
lidwe labwino.
Chitsanzo: Makolo akamapanda kukwapula mwana, mwa-
nayo amakula mopulukira ngati nkhuku yavetenale.
Kukula movutikira: Kukula ndi moyo wovuta kwambiri.
Chitsanzo: Ana amene anakula movutikira amakhala
opanda chibwana.
Kukula mtima: Kuchita makani.
Chitsanzo: Kuno sitifuna mwana wokula mtima.
Kukula mutu: Kusowa chochita.
Chitsanzo: (1) Mutu wanga wakula, ndikusowa choti
ndingachite. (2) Mavuto akakugwera umakula mutu.
Kukulira m’chitukutuku: Kukula mopusa.
Chitsanzo: Ana omwe anakulira m’chitukutuku,
amalephera ndi kuphika komwe.
Kukulowa: Kukuzolowera kwambiri, kusiya kukupats ale-
mu.
Chitsanzo: Anthu amenewa asandilowe chonchoyi!
Kukulunga nsima: Kuphika nsima.
Chitsanzo: Koma ndiye nsimayi mwaikulungatu.
146