Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 141

Paphata pa Chichewa Kukhomera kudowa: Kusabereka. Chitsanzo: Ambiri akaona kuti wina m’banja anakhomera kudowa, amatuluka m’nyumba n’kupita kwina, kapena kulowetsa fisi. Kukhomereza: Kuthandiza wina kuti zimene ukumuuza zimulowe mumtima, azimvetse. Chitsanzo: Mawu awa muziwakhomereza mwa ana anu. Kukhosi kuli bii: (a) Usakusangalala. Chitsanzo: Ndimadya nsimayo kukhosi kuli bii. (b) Kuda nkhawa. Chitsanzo: Nditangomva za nkhaniyo ndinangoti kukhosi bii. Kukhudula: Kumenya mwankhanza. Chitsanzo: (1) Ukandiputanso ndikukhudula. (2) Akungomwaza ndalama. Zikuoneka kuti wakatamuka. Kukhudza mtima: Kukhudzika, kukhala ndi chisoni. Chitsanzo: Nkhani imeneyi yandikhudza mtima. Kukhudza: (a) Kukhala ndi mlandu, kupezeka kuti unachita nawo kapena ukufunika kuyankha pa nkhani inayake chifukwa cha zimene unachita. Chitsanzo: Atandiuza kuti nkhaniyo ikundikhudza ndinawakanira kuti sikundikhudza. (b) Kugwira chinthu. Chitsanzo: Ndachulutsa masamba kuti ndisakhudze nyansi. (c) Kukhala pachisoni chifukwa cha maliro kapena vuto lina lalikulu, kusiya zochita zina posonyeza chisoni. 140