Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 139

Paphata pa Chichewa Kukhala moyo wosalira zambiri: Kukhutira ndi zochepa zimene uli nazo, kusakhala ndi chuma chambiri. Chitsanzo: Anthu amene amakhala moyo wosalira zambiri amasangalala. Kukhala ndwii ngati akukumeta: Kukhala chete. Chitsanzo: Musangotitu ndwii ngati akukumentani apa! Kukhala phwi: Kungokhala pansi ngati chithumba. Chitsanzo: Usangokhala phwi apa, tadzuka. Kukhala thako limodzi: Kukhala mosakhazikika. Chitsanzo: Pamudzi pano tangokhala thako limodzi. Kukhala thako limodzi: Kusakhazikika. Chitsanzo: Ife pamudzi pano tangokhala thako limodzi. Kukhala: Kugwirizana ndi thupi lako, zinthu zomwe zimaoneka bwino zikakhala limodzi, chinthu chomwe ukachivala umaoneka nacho bwino. Tanthauzo lake le- nileni ndi ndi kukhazika thupi pansi. Chitsanzo: (1) Chovalachi chikukukhalani. (2) Akazi awo aja amawakhala. Kukhalira kulimba: Kukhala movutika kwambiri. Chitsanzo: Moyowu ndi wovuta moti tikungokhalira kulim- ba. Kukhalira kupirira: Kukhala mozunzika. Chitsanzo: Ukayamba kuona kuti pabanja ukukhalira kupirira, umafunika kukumbukira kuti palibe anakutuma kuti umulole. Kukhalira manja: Kungokhala osachita chilichonse. Chitsanzo: Ukakhalira manja udyanji? 138